Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 15:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Tsopano Puli+ mfumu ya Asuri+ inabwera m’dzikomo. Choncho Menahemu anapatsa+ Puli matalente* 1,000 a siliva,+ kuti amuthandize kulimbitsa ufumu umene unali m’manja mwake.+

  • 2 Mafumu 16:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Chotero Ahazi anatumiza amithenga kwa Tigilati-pilesere+ mfumu ya Asuri ndi uthenga wakuti: “Ndine mtumiki wanu+ ndi mwana wanu. Bwerani mudzandipulumutse+ m’manja mwa mfumu ya Siriya ndi m’manja mwa mfumu ya Isiraeli, amene akundiukira.”

  • 2 Mafumu 17:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Iye ndiye amene Salimanesere+ mfumu ya Asuri+ anabwera kudzamuthira nkhondo. Chotero Hoshiya anakhala mtumiki wake n’kuyamba kupereka msonkho+ kwa iye.

  • Yeremiya 2:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Ndiyeno n’chifukwa chiyani ukufuna kuyenda m’njira ya ku Iguputo+ kuti ukamwe madzi a mumtsinje wa Sihori?+ N’chifukwa chiyani ukufuna kuyenda m’njira yopita kudziko la Asuri+ kuti ukamwe madzi a mumtsinje wa Firate?

  • Yeremiya 2:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 N’chifukwa chiyani kusintha njira kwako ukukuona mopepuka?+ Udzachitanso manyazi ndi Iguputo+ monga mmene unachitira manyazi ndi Asuri.+

  • Maliro 5:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Kuti tipeze chakudya chokwanira, tikudalira Iguputo+ ndi Asuri.+

  • Ezekieli 16:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 “‘Unachitanso uhule ndi ana aamuna a Asuri chifukwa chakuti sunali kukhutira.+ Unapitiriza kuchita nawo uhule koma sunakhutirebe.

  • Hoseya 5:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Efuraimu anaona kudwala kwake ndipo Yuda anaona chilonda chake.+ Pamenepo Efuraimu anapita ku Asuri+ ndipo anatumiza amithenga kwa mfumu yaikulu.+ Koma mfumuyo sinathe kukuchiritsani anthu inu,+ ndipo sinathe kupoletsa chilonda chanu.+

  • Hoseya 7:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Efuraimu ali ngati nkhunda yopusa,+ yopanda nzeru.+ Iwo apempha thandizo ku Iguputo+ ndiponso apita kudziko la Asuri.+

  • Hoseya 8:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iwo apita kudziko la Asuri+ ngati mbidzi yoyenda yokha.+ Koma Efuraimu walipira akazi kuti azigona nawo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena