Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 34:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndipo Yehova anadutsa pamaso pa Mose akulengeza kuti: “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo+ ndi wachisomo,+ wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha+ ndi choonadi.+

  • Numeri 14:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 ‘Yehova ndi wosakwiya msanga,+ ndipo ndi wodzaza ndi kukoma mtima kosatha.+ Amakhululukira wolakwa ndi wophwanya malamulo,+ koma iye salekerera konse wolakwa osam’langa.+ Amalanga ana, zidzukulu, ndi ana a zidzukuluzo chifukwa cha zolakwa za makolo awo.’+

  • Deuteronomo 32:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,+

      Ndipo adzamva chisoni chifukwa cha atumiki ake,+

      Chifukwa adzaona kuti thandizo lawachokera.

      Adzaona kuti pangokhala munthu wonyozeka ndi wopanda pake.

  • Oweruza 2:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Yehova akawapatsa oweruza,+ Yehova anali kukhaladi ndi aliyense wa oweruzawo, ndipo iye anali kuwapulumutsa m’manja mwa adani awo masiku onse a moyo wa woweruzayo. Yehova anali kuchita zimenezo pakuti anali kuwamvera chisoni+ akamva kubuula kwawo chifukwa cha owapondereza ndi owakankhakankha.+

  • 2 Samueli 24:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Ndiyeno mngelo+ anali atatambasula dzanja lake kuloza ku Yerusalemu kuti awononge mzindawo. Pamenepo Yehova anamva chisoni+ chifukwa cha tsokalo, choncho anauza mngelo amene anali kupha anthuyo kuti: “Basi pakwanira! Tsopano tsitsa dzanja lako.” Pa nthawiyi, mngelo wa Yehova uja anali pafupi ndi malo opunthira mbewu a Arauna+ Myebusi.+

  • Salimo 51:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 51 Ndikomereni mtima inu Mulungu, malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha.+

      Malinga ndi kuchuluka kwa chifundo chanu, fafanizani zolakwa zanga.+

  • Salimo 69:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Ndiyankheni inu Yehova, pakuti kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwabwino.+

      Ndicheukireni chifukwa chifundo chanu ndi chochuluka,+

  • Salimo 86:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Koma inu Yehova, ndinu Mulungu wachifundo ndi wachisomo,+

      Wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha ndi choonadi.+

  • Salimo 90:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Bwererani kwa ife, inu Yehova!+ Kodi mudzatenga nthawi yaitali bwanji musanabwerere kwa ife?+

      Timvereni chisoni ife atumiki anu.+

  • Yesaya 63:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndidzanena za ntchito za Yehova zosonyeza kukoma mtima kwake kosatha.+ Ndidzatamanda Yehova, mogwirizana ndi zonse zimene Yehova watichitira.+ Ndidzauza nyumba ya Isiraeli zabwino zochuluka+ zimene iye wawachitira chifukwa cha chifundo chake,+ komanso chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha ndiponso kwakukulu.

  • Maliro 3:32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Ngakhale kuti watichititsa kumva chisoni,+ ndithu adzatichitira chifundo chifukwa kukoma mtima kwake kosatha n’kwakukulu.+

  • Yoweli 2:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ng’ambani mitima yanu+ osati zovala zanu+ ndipo bwererani kwa Yehova Mulungu wanu pakuti iye ndi wachisomo, wachifundo,+ wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha.+ Ndithu, iye adzakumverani chisoni chifukwa cha tsokalo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena