Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yoswa 13:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 (Dera loyambira kukamtsinje kotuluka mu Nailo kum’mawa kwa Iguputo, kukafika kumpoto kumalire ndi Ekironi,+ ankalitcha dziko la Akanani.)+ Madera a Afilisitiwa akulamulidwa ndi olamulira ogwirizana asanu.+ Maderawo ndi Gaza,+ Asidodi,+ Asikeloni,+ Gati+ ndi Ekironi,+ komanso Aavi+ akukhala komweko.

  • Oweruza 3:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Mitunduyo ndi olamulira asanu ogwirizana+ a Afilisiti,+ Akanani onse,+ ngakhalenso Asidoni+ ndi Ahivi+ okhala m’phiri la Lebanoni,+ kuchokera kuphiri la Baala-herimoni+ mpaka kumalire a dera la Hamati.+

  • Oweruza 16:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Pamenepo olamulira ogwirizana+ a Afilisiti anafika kwa mkaziyo ndi kumuuza kuti: “Umunyengerere+ kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zazikuluzo ndi zimene tingachite kuti timugonjetse. Ufufuzenso zimene tingam’mange nazo kuti tithane naye. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva zokwana 1,100.”+

  • Oweruza 16:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Ndipo Samisoni anati: “Ndife nawo limodzi+ Afilisitiwa.” Pamenepo anawerama atasonkhanitsa mphamvu zake zonse moti nyumbayo inagwera olamulira ogwirizana a Afilisiti ndi anthu onse amene anali m’nyumbayo.+ Anthu amene Samisoni anawapha pa imfa yake anali ambiri kuposa anthu amene anawapha pa moyo wake.+

  • 1 Samueli 5:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Chotero anatumiza uthenga ndi kusonkhanitsa olamulira onse ogwirizana a Afilisiti ku Asidodi ndi kuwauza kuti: “Tichite nalo chiyani likasa la Mulungu wa Isiraeli?” Pamapeto pake iwo anati: “Likasa limeneli la Mulungu wa Isiraeli tilitumize kumzinda wa Gati.”+ Choncho anapititsa likasa la Mulungu wa Isiraeli kumeneko atayenda nalo mozungulira.

  • 1 Samueli 6:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ndiyeno iwo anafunsa kuti: “Kodi nsembe ya kupalamula imene tiyenera kupereka ikhale chiyani?” Poyankha, ansembe ndi alauli aja anati: “Mupereke zifanizo zisanu zagolide za matenda a mudzi, ndi zifanizo zisanu zagolide za mbewa zoyenda modumpha, malinga ndi chiwerengero cha olamulira ogwirizana+ a Afilisiti. Muchite zimenezi pakuti mliri umene wagwera aliyense wa inu, pamodzi ndi olamulira anu ogwirizana ndi umodzi.

  • 1 Samueli 29:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Olamulira ogwirizana+ a Afilisiti anali kudutsa m’magulu a asilikali 100, ndi 1,000, ndipo Davide ndi amuna amene anali kuyenda naye anadutsa pambuyo pawo limodzi ndi Akisi.+

  • 1 Mbiri 12:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Analiponso ena a fuko la Manase amene anapanduka n’kupita kwa Davide pamene iye anabwera ndi Afilisiti+ kudzamenyana ndi Sauli. Koma Davide sanawathandize Afilisitiwo chifukwa olamulira awo ogwirizana+ atakambirana, anam’bweza chifukwa anati: “Ameneyu akhoza kukatitembenukira n’kugwirizana ndi mbuye wake Sauli, kenako akatidula mitu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena