1 Mbiri
3 Ana amene Davide+ anabereka ku Heburoni+ anali awa: woyamba Aminoni,+ wobadwa kwa Ahinowamu+ wa ku Yezereeli,+ wachiwiri Danieli, wobadwa kwa Abigayeli+ wa ku Karimeli,+ 2 wachitatu Abisalomu,+ wobadwa kwa Maaka+ mwana wamkazi wa Talimai+ mfumu ya Gesuri,+ wachinayi Adoniya,+ wobadwa kwa Hagiti,+ 3 wachisanu Sefatiya, wobadwa kwa Abitali,+ wa 6 Itireamu, wobadwa kwa Egila+ mkazi wake. 4 Davide anabereka ana 6 ku Heburoni ndipo analamulira kumeneko zaka 7 ndi miyezi 6. Kenako analamulira zaka 33 ku Yerusalemu.+
5 Ku Yerusalemu+ iye anabereka ana awa: Simeya,+ Sobabu,+ Natani,+ ndi Solomo,+ ana anayi obadwa kwa Bati-seba+ mwana wamkazi wa Amiyeli.+ 6 Anaberekanso Ibara,+ Elisama,+ Elifeleti,+ 7 Noga, Nefegi, Yafiya,+ 8 Elisama,+ Eliyada, ndi Elifeleti,+ ana 9. 9 Amenewa ndiwo anali ana onse a Davide, kuwonjezera pa ana a adzakazi ake, ndipo Tamara+ anali mlongo wawo.
10 Mwana wa Solomo anali Rehobowamu.+ Rehobowamu anabereka Abiya,+ Abiya anabereka Asa,+ Asa anabereka Yehosafati,+ 11 Yehosafati anabereka Yehoramu,+ Yehoramu anabereka Ahaziya,+ Ahaziya anabereka Yehoasi,+ 12 Yehoasi anabereka Amaziya,+ Amaziya anabereka Azariya,+ Azariya anabereka Yotamu,+ 13 Yotamu anabereka Ahazi,+ Ahazi anabereka Hezekiya,+ Hezekiya anabereka Manase,+ 14 Manase anabereka Amoni,+ ndipo Amoni anabereka Yosiya.+ 15 Ana a Yosiya anali awa: woyamba Yohanani, wachiwiri Yehoyakimu,+ wachitatu Zedekiya,+ ndipo wachinayi anali Salumu. 16 Mwana wa Yehoyakimu anali Yekoniya.+ Yekoniya anabereka Zedekiya. 17 Ana amene Yekoniya anabereka ali mkaidi anali Salatiyeli,+ 18 Malikiramu, Pedaya, Senazara, Yekamiya, Hosama, ndi Nedabiya. 19 Ana a Pedaya anali Zerubabele+ ndi Simeyi. Ana a Zerubabele anali Mesulamu ndi Hananiya, (Selomiti anali mlongo wawo), 20 Hasuba, Oheli, Berekiya, Hasadiya, ndi Yusabi-hesedi, ana asanu. 21 Ana a Hananiya anali Pelatiya+ ndi Yesaiya, mwana wa Yesaiya anali Refaya, mwana wa Refaya anali Arinani, mwana wa Arinani anali Obadiya, mwana wa Obadiya anali Sekaniya, 22 mwana wa Sekaniya anali Semaya, ndipo ana a Semaya anali Hatusi, Igali, Bariya, Neariya, ndi Safati, ana 6. 23 Ana a Neariya anali Elioenai, Hizikiya, ndi Azirikamu, ana atatu. 24 Ana a Elioenai anali Hodaviya, Eliyasibu, Pelaya, Akubu, Yohanani, Delaya, ndi Anani, ana 7.