Yohane
3 Tsopano panali Mfarisi wina dzina lake Nikodemo,+ wolamulira wa Ayuda. 2 Iyeyu anabwera kwa Yesu usiku+ ndi kumuuza kuti: “Rabi,+ tikudziwa kuti inu ndinu mphunzitsi+ wochokera kwa Mulungu,+ chifukwa munthu sangathe kuchita zizindikiro+ zimene inu mumachita ngati Mulungu sali naye.”+ 3 Poyankha Yesu anati:+ “Ndithudi ndikukuuza, Munthu sangathe kuona ufumu wa Mulungu atapanda kubadwanso.”+ 4 Nikodemo anafunsa kuti: “Munthu angabadwe bwanji ali wamkulu kale? Kodi angathe kulowa m’mimba mwa mayi ake ndi kubadwanso?” 5 Yesu anayankha kuti: “Ndithudi ndikukuuza, Munthu sangathe kulowa mu ufumu wa Mulungu atapanda kubadwa mwa madzi+ ndi mzimu.+ 6 Chobadwa mwa thupi n’chanyama, ndipo chobadwa mwa mzimu n’chauzimu.+ 7 Usadabwe chifukwa ndakuuza kuti, Anthu inu muyenera kubadwanso.+ 8 Mphepo+ imawombera kumene ikufuna, ndipo munthu amamva mkokomo wake, koma sadziwa kumene ikuchokera ndi kumene ikupita. N’chimodzimodzinso aliyense wobadwa mwa mzimu.”+
9 Poyankha Nikodemo anati: “Zimenezi zingatheke bwanji?” 10 Yesu anamufunsa kuti: “Kodi iwe sudziwa zinthu zimenezi, chikhalirecho ndiwe mphunzitsi wa Isiraeli?+ 11 Ndithudi ndikukuuza, Zimene ife timadziwa timazilankhula, ndipo zimene taona timazichitira umboni.+ Koma anthu inu simulandira umboni umene timapereka.+ 12 Ngati ndakuuzani zinthu za padziko lapansi koma inu osakhulupirira, mudzakhulupirira bwanji ndikakuuzani zinthu zakumwamba?+ 13 Ndipo palibe munthu amene anakwera kumwamba+ koma Mwana wa munthu+ yekha, amene anatsika kuchokera kumwambako.+ 14 Ndiponso, monga mmene Mose anakwezera njoka m’mwamba+ m’chipululu, momwemonso Mwana wa munthu ayenera kukwezedwa m’mwamba,+ 15 kuti aliyense wokhulupirira iye akhale nawo moyo wosatha.+
16 “Pakuti Mulungu anakonda+ kwambiri dziko mwakuti anapereka Mwana wake wobadwa yekha,+ kuti aliyense wokhulupirira+ iye asawonongeke,+ koma akhale ndi moyo wosatha.+ 17 Pakuti Mulungu anatumiza Mwana wake m’dziko, osati kuti mwanayo adzaweruze+ dziko, koma kuti mwa iye, dziko lipulumutsidwe.+ 18 Wokhulupirira mwa iye sayenera kuweruzidwa.+ Wosakhulupirira waweruzidwa kale, chifukwa sanakhulupirire m’dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.+ 19 Tsopano maziko operekera chiweruzo ndi awa, kuwala+ kwafika m’dziko+ koma anthu akonda mdima m’malo mwa kuwala,+ pakuti ntchito zawo n’zoipa. 20 Amene amachita zinthu zoipa+ amadana ndi kuwala ndipo safika pamene pali kuwala, kuti ntchito zake zisadzudzulidwe.+ 21 Koma amene amachita chimene chili chabwino amabwera pamene pali kuwala,+ kuti ntchito zake zionekere kuti anazichita mogwirizana ndi chifuniro cha Mulungu.”
22 Izi zitatha, Yesu ndi ophunzira ake anapita m’dera la Yudeya, ndipo anakhala nawo kumeneko ndi kubatiza anthu.+ 23 Koma Yohane+ analinso kubatiza ku Ainoni pafupi ndi Salimu, chifukwa kunali madzi ambiri+ kumeneko, ndipo anthu anali kubwera kudzabatizidwa.+ 24 Pa nthawiyi n’kuti Yohane asanaponyedwe m’ndende.+
25 Tsopano ophunzira a Yohane anayambitsa mkangano ndi Myuda wina pa nkhani yokhudza mwambo wa kuyeretsa.+ 26 Pamenepo anafika kwa Yohane ndi kumuuza kuti: “Rabi, munthu amene munali naye kutsidya kwa Yorodano uja, amene munali kumuchitira umboni uja,+ iyenso akubatiza ndipo anthu onse akupita kwa iye.”+ 27 Poyankha Yohane anati: “Munthu sangalandire kanthu kalikonse akapanda kupatsidwa kuchokera kumwamba.+ 28 Inu nomwe ndinu mboni zanga pamawu amene ndinanena kuti, Ine sindine Khristu,+ koma, ndinatumizidwa monga kalambulabwalo wake.+ 29 Iye amene ali ndi mkwatibwi ndiye mkwati.+ Koma mnzake wa mkwati, akaimirira ndi kumvetsera zimene akunena, amakhala n’chimwemwe chochuluka chifukwa cha mawu a mkwatiyo. Choncho chimwemwe changa chasefukiradi.+ 30 Ameneyo ayenera kumawonjezereka, koma ine ndiyenera kucheperachepera.”
31 Wochokera kumwamba ali woposa ena onse.+ Wochokera padziko lapansi ndi wa padziko lapansi, ndipo amalankhula zinthu za padziko lapansi.+ Koma wochokera kumwamba ali woposa ena onse.+ 32 Zimene iye waziona ndi kuzimva, akuchitira umboni zimenezo,+ koma palibe munthu amene akulandira umboni wake.+ 33 Amene walandira umboni wakewo waika chisindikizo chake pa umboniwo chakuti Mulungu amanena zoona.+ 34 Wotumidwa ndi Mulungu amalankhula mawu a Mulungu,+ pakuti akafuna kupereka mzimu sachita kuyeza pamuyezo.+ 35 Atate amakonda Mwana wake+ ndipo anapereka zinthu zonse m’manja mwake.+ 36 Iye wokhulupirira+ mwa Mwanayo ali nawo moyo wosatha.+ Wosamvera Mwanayo sadzauona moyowu,+ koma mkwiyo wa Mulungu ukhalabe pa iye.+