Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 18:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 “‘Usalole kuti aliyense mwa ana ako aperekedwe+ kwa Moleki.*+ Usanyoze+ dzina la Mulungu wako mwa njira imeneyi. Ine ndine Yehova.+

  • 2 Mafumu 16:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Anayenda m’njira ya mafumu a ku Isiraeli,+ ndipo ngakhale mwana wake wamwamuna anamuwotcha* pamoto,+ mofanana ndi zonyansa+ za anthu a mitundu ina amene Yehova anawapitikitsa chifukwa cha ana a Isiraeli.

  • 2 Mafumu 17:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Iwo anapitiriza kuwotcha* pamoto+ ana awo aamuna ndi aakazi, kulosera+ ndi kuwombeza.*+ Anapitirizanso+ kuchita zoipa* pamaso pa Yehova ndi cholinga chomukwiyitsa.+

  • 2 Mafumu 21:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Manase anatentha* mwana wake wamwamuna pamoto,+ ndipo ankachita zamatsenga,+ ankawombeza,*+ ndiponso anaika anthu olankhula ndi mizimu ndi olosera+ zam’tsogolo. Iye anachita zinthu zambiri zoipa pamaso pa Yehova ndiponso zomukwiyitsa.

  • 2 Mbiri 28:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ahazi anafukiza nsembe yautsi+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu.+ Iye anawotcha ana ake+ pamoto mofanana ndi zonyansa+ za anthu a mitundu ina amene Yehova anawapitikitsa pamaso pa ana a Isiraeli.+

  • 2 Mbiri 33:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Manase anatentha* ana ake aamuna pamoto+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ ndipo ankachita zamatsenga,+ ankawombeza,+ ankachita zanyanga,+ ndiponso anaika anthu olankhula ndi mizimu+ ndi olosera zam’tsogolo.+ Iye anachita zinthu zambiri zoipa pamaso pa Yehova ndiponso zomukwiyitsa.+

  • Yeremiya 7:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Iwo amanga malo okwezeka ku Tofeti,+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ kuti azitentha ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto,+ chinthu chimene sindinawalamule kuchita ndiponso chimene sindinachiganizirepo mumtima mwanga.’+

  • Yeremiya 19:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Iwo amangiranso Baala malo okwezeka kuti azitentherapo ana awo aamuna monga nsembe zopsereza zathunthu zoperekedwa kwa Baala.+ Ine sindinawalamule zimenezi kapena kuzitchula,+ ndipo sindinaziganizirepo mumtima mwanga.”’+

  • Yeremiya 32:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Kuwonjezera apo anamangira Baala+ malo okwezeka m’chigwa cha mwana wa Hinomu.+ Anachita izi kuti azidutsitsa ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto monga nsembe+ kwa Moleki.+ Ine sindinawalamule zimenezi+ ndipo sindinaganizirepo mumtima mwanga kuchita chinthu chonyansa chimenechi,+ kuti Yuda achite tchimo.’+

  • Ezekieli 16:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “‘Unali kutenga ana ako aamuna ndi aakazi amene unandiberekera+ n’kumawapereka nsembe kwa mafano.+ Kodi zochita zako zauhulezo sizinakukwanire?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena