Mateyu
23 Pambuyo pake Yesu analankhula kwa khamu la anthu ndi kwa ophunzira ake+ kuti: 2 “Alembi+ ndi Afarisi adzikhazika pampando wa Mose.+ 3 Chotero muzichita ndi kutsatira zilizonse zimene angakuuzeni,+ koma musamachite zimene iwo amachita,+ chifukwa iwo amangonena koma osachita. 4 Iwo amamanga akatundu olemera ndi kusenzetsa anthu pamapewa,+ koma eni akewo safuna kusuntha akatunduwo ndi chala chawo.+ 5 Zonse zimene amachita, amazichita kuti anthu awaone.+ Iwo amakulitsa timapukusi tokhala ndi malemba+ timene amavala monga zodzitetezera, ndipo amakulitsanso ulusi wopota wa m’mphepete+ mwa zovala zawo. 6 Amakonda malo olemekezeka kwambiri+ pa chakudya chamadzulo ndi mipando yakutsogolo m’masunagoge.+ 7 Amakondanso kupatsidwa moni+ m’misika komanso kuti anthu aziwatchula kuti Rabi.+ 8 Koma inu musamatchulidwe kuti Rabi, chifukwa mphunzitsi wanu ndi mmodzi yekha,+ ndipo nonsenu ndinu abale. 9 Komanso musamatchule aliyense kuti atate wanu padziko lapansi pano, pakuti Atate wanu ndi mmodzi,+ wakumwamba Yekhayo. 10 Musamatchedwe ‘atsogoleri,’+ pakuti Mtsogoleri wanu ndi mmodzi, Khristu. 11 Koma wamkulu kwambiri pakati panu akhale mtumiki wanu.+ 12 Aliyense wodzikweza adzatsitsidwa,+ koma aliyense wodzichepetsa adzakwezedwa.+
13 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mukutseka+ ufumu wakumwamba kuti anthu asalowemo. Pakuti inuyo+ simukulowamo, mukuletsa amene akufuna kulowamo kuti asalowe. 14* ——
15 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu!+ Chifukwa mumatha mitunda kuti mukatembenuze munthu mmodzi, koma akatembenuka mumam’sandutsa woyenera kuponyedwa m’Gehena* kuposa inuyo.
16 “Tsoka kwa inu atsogoleri akhungu,+ amene mumati, ‘Ngati munthu walumbirira kachisi palibe kanthu, koma ngati munthu walumbirira golide wa m’kachisi, asunge lumbiro lake.’+ 17 Opusa ndi akhungu inu! Chofunika kwambiri n’chiti, golide kapena kachisi amene wayeretsa golideyo?+ 18 Komanso mumati, ‘Ngati munthu walumbirira guwa lansembe, palibe kanthu, koma ngati munthu walumbirira mphatso imene ili paguwapo, asunge lumbiro lake.’ 19 Akhungu inu! Chofunika kwambiri n’chiti, mphatso kapena guwa lansembe+ limene limayeretsa mphatsoyo? 20 Chotero amene walumbirira guwa lansembe walumbirira guwalo ndi zonse zimene zili pamenepo, 21 ndipo amene walumbirira kachisi walumbirira kachisiyo limodzi ndi iye amene amakhala mmenemo.+ 22 Wolumbirira kumwamba walumbirira mpando wachifumu wa Mulungu+ komanso amene akukhala pampandowo.
23 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mumapereka chakhumi+ cha timbewu ta minti, dilili, ndi chitowe, koma mumanyalanyaza zinthu zofunika za m’Chilamulo, monga chilungamo,+ chifundo+ ndi kukhulupirika.+ Kupereka zinthu zimenezi n’kofunikadi, koma osanyalanyaza zinthu zinazo. 24 Atsogoleri akhungu inu,+ amene mumasefa zakumwa zanu kuti muchotsemo kanyerere+ koma mumameza ngamila.+
25 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mumayeretsa kunja kwa kapu+ ndi mbale, koma mkati mwake mutadzaza zolanda+ ndi kusadziletsa. 26 Mfarisi wakhungu+ iwe, yeretsa mkati mwa kapu+ ndi mbale choyamba, kuti kunja kwakenso kukhale koyera.
27 “Tsoka inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu!+ Chifukwa mumafanana ndi manda opaka laimu,+ amene kunja kwake amaonekadi okongola, koma mkati mwake muli mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zamitundu yonse. 28 Mofanana ndi zimenezi inunso, pamaso pa anthu, mumaonekadi ngati olungama+ koma mkati mwanu mwadzaza chinyengo ndi kusamvera malamulo.
29 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu!+ Chifukwa mumamanga manda a aneneri ndi kukongoletsa manda achikumbutso a anthu olungama,+ 30 ndipo mumanena kuti, ‘Tikanakhalako m’masiku a makolo athu, ifeyo sitikanakhudzidwa ndi mlandu wawo wokhetsa magazi a aneneri.’+ 31 Chotero mukudzichitira nokha umboni kuti ndinu ana a anthu amene anapha aneneri.+ 32 Choncho malizitsani ntchito+ imene makolo anu anayamba.
33 “Njoka inu, ana a mphiri,+ mudzathawa bwanji chiweruzo cha Gehena?+ 34 Pa chifukwa chimenechi, tsopano ndikukutumizirani+ aneneri, anthu anzeru ndi aphunzitsi.+ Ena a iwo mudzawapha+ ndi kuwapachika, ndipo ena mudzawakwapula+ m’masunagoge mwanu ndi kuwazunza mumzinda ndi mzinda, 35 kuti magazi onse olungama okhetsedwa padziko lapansi abwere pa inu,+ kuyambira magazi a Abele+ wolungama+ mpaka magazi a Zekariya mwana wa Barakiya, amene inu munamupha pakati pa nyumba yopatulika ndi guwa lansembe.+ 36 Ndithu ndikukuuzani kuti, Zinthu zonsezi zidzaubwerera m’badwo uwu.+
37 “Yerusalemu, Yerusalemu, wakupha aneneri iwe+ ndi woponya miyala+ anthu otumizidwa kwa iwe.+ Mobwerezabwereza ndinafuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, muja nkhuku yathadzi imasonkhanitsira anapiye ake m’mapiko.+ Koma anthu inu simunafune zimenezo.+ 38 Tsopano tamverani! Mulungu wachoka n’kukusiyirani+ nyumba* yanuyi.+ 39 Ndithu ndikukuuzani, Kuyambira tsopano simudzandionanso kufikira pamene mudzanene kuti, ‘Wodalitsidwa iye wobwera m’dzina la Yehova!’”+