Yeremiya
48 Ponena za Mowabu,+ Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti:
“Tsoka Nebo+ chifukwa wawonongedwa!
Kiriyataimu+ wachititsidwa manyazi ndipo walandidwa.
Malo othawirako otetezeka* achititsidwa manyazi ndipo awonongedwa.+
2 Mowabu sakutamandidwanso.
Ku Hesiboni+ adani amukonzera chiwembu kuti amuwononge ndipo akunena kuti:
‘Bwerani, tiyeni timuwononge kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’
Iwenso Madimeni khala chete,
Chifukwa lupanga likukutsatira.
4 Mowabu wawonongedwa.
Ana ake akulira.
5 Anthu akulira mosalekeza pamene akukwera zitunda za Luhiti.
Ndipo panjira yochokera ku Horonaimu akumva anthu akulira mowawidwa mtima chifukwa cha tsoka limene lawagwera.+
6 Thawani, pulumutsani moyo wanu!
Mukhale ngati mtengo wa junipa* mʼchipululu.
7 Chifukwa chakuti mukudalira ntchito zanu ndi chuma chanu,
Inunso mudzagwidwa ndi adani.
Ndipo Kemosi+ adzatengedwa kupita ku ukapolo
Pamodzi ndi ansembe ake ndi akalonga ake.
Chigwa chidzawonongedwa,
Chimodzimodzinso malo afulati,* mogwirizana ndi zimene Yehova wanena.
9 Perekani chizindikiro chapamsewu kwa anthu a ku Mowabu,
Chifukwa adzathawa pamene dziko lawo likusanduka bwinja,
Ndipo mizinda yake idzakhala chinthu chochititsa mantha,
Moti simudzapezeka aliyense wokhalamo.+
10 Munthu wozengereza kugwira ntchito imene Yehova wamupatsa ndi wotembereredwa.
Munthu wopewa kukhetsa magazi ndi lupanga lake ndi wotembereredwa.
11 Anthu a ku Mowabu akhala popanda wowasokoneza kuyambira pa unyamata wawo
Ngati vinyo amene nsenga zake zadikha.
Iwo sanatsanulidwepo kuchoka mʼchiwiya china kupita mʼchiwiya china,
Ndipo sanapitepo ku ukapolo.
Nʼchifukwa chake kukoma kwawo sikunasinthe,
Ndipo fungo lawo silinasinthenso.
12 ‘Choncho masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzawatumizire anthu kuti awapendeketse. Adzawapendeketsa nʼkuwakhuthula ngati vinyo mʼziwiya zawo ndipo adzaswa mitsuko yawo ikuluikulu kukhala mapalemapale. 13 Amowabuwo adzachita manyazi ndi Kemosi, ngati mmene anthu a mʼnyumba ya Isiraeli achitira manyazi ndi Beteli, mzinda umene ankaudalira.+
14 Nʼchifukwa chiyani mukunena kuti: “Ndife asilikali amphamvu, okonzeka kumenya nkhondo”?’+
Ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+
17 Onse owazungulira adzawamvera chisoni,
Onse amene akudziwa dzina lawo.
Auzeni kuti: ‘Taonani mmene ndodo yamphamvu ndi yokongola ija yathyokera!’
18 Tsika pamalo ako aulemerero
Ndipo ukhale pansi uli ndi ludzu,* iwe mwana wamkazi wokhala ku Diboni+
Chifukwa wowononga Mowabu wabwera kudzakuukira,
Ndipo malo ako a mipanda yolimba kwambiri adzawasandutsa bwinja.+
19 Iwe amene ukukhala ku Aroweli, ima mʼmbali mwa msewu ndipo uone zimene zikuchitika.+
Funsa mwamuna ndi mkazi amene akuthawa kuti, ‘Chachitika nʼchiyani?’
20 Mowabu wachititsidwa manyazi ndipo wagwidwa ndi mantha aakulu.
Lirani mofuula.
Lengezani ku Arinoni+ kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Chiweruzo chafika padziko lafulati.*+ Chafika ku Holoni, Yahazi,+ Mefaata,+ 22 Diboni,+ Nebo,+ Beti-dibilataimu, 23 Kiriyataimu,+ Beti-gamuli, Beti-meoni,+ 24 Kerioti,+ Bozira ndi mizinda yonse yamʼdziko la Mowabu, yakutali ndi yapafupi.
26 ‘Muledzeretseni+ chifukwa wadzikuza pamaso pa Yehova.+
Mowabu akugubuduka mʼmasanzi ake,
Ndipo wakhala chinthu choyenera kuchinyoza.
27 Kodi kwa inu, Isiraeli sanali chinthu choyenera kunyozedwa?+
Kodi anapezeka pakati pa anthu akuba,
Kuti inu mumupukusire mitu nʼkumamunenera zinthu zoipa?
28 Inu anthu okhala ku Mowabu, chokani mʼmizinda ndipo mukakhale pathanthwe.
Mukhale ngati njiwa imene imamanga chisa chake mʼmbali mwa khomo la phanga.’”
29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu. Iye ndi wodzikuza kwambiri.
Tamva za kudzitukumula kwake, kunyada kwake, kudzikweza kwake ndi kudzikuza kwa mtima wake.”+
30 “‘Ine ndikudziwa za mkwiyo wake,’ akutero Yehova,
‘Koma mawu ake opanda pakewo sadzakwaniritsidwa.
Iwo sadzachita chilichonse.
31 Nʼchifukwa chake Mowabu ndidzamulirira,
Mowabu yense ndidzamulirira mofuula
Ndipo ndidzalira maliro a amuna a ku Kiri-haresi.+
Mphukira zako zosangalala zawoloka nyanja.
Zafika kunyanja, ku Yazeri.
Ndachititsa kuti vinyo asiye kutuluka moponderamo mphesa.
Palibe amene adzapondeponde mphesa akufuula mosangalala.
Padzamveka kufuula koma osati kwachisangalalo.’”+
34 “‘Kulira kochokera ku Hesiboni+ kukumveka ku Eleyale.+
Kulira kwawo kukumveka mpaka ku Yahazi,+
Kukumveka kuchokera ku Zowari kukafika ku Horonaimu+ ndi ku Egilati-selisiya.
Ngakhale madzi a ku Nimurimu adzauma.+
35 Ndidzachititsa kuti mʼdziko la Mowabu musapezeke
Munthu aliyense wobweretsa nsembe kumalo okwezeka
Komanso munthu wopereka nsembe kwa mulungu wake,’ akutero Yehova.
36 ‘Nʼchifukwa chake mtima wanga udzalirire* Mowabu ngati chitoliro,*+
Mtima wanga udzalirira* amuna a ku Kiri-haresi ngati chitoliro.*
Chifukwa chuma chimene wapanga chidzawonongeka.
Akulira chifukwa ndaphwanya Mowabu
Ngati chiwiya choyenera kutaidwa,’ akutero Yehova.
39 ‘Taonani, Mowabu wachita mantha kwambiri. Lirani mofuula!
Mowabu wabwerera mwamanyazi.
Mowabu wasanduka chinthu choyenera kunyozedwa,
Komanso chochititsa mantha kwa anthu onse amene amuzungulira.’
40 Yehova wanena kuti:
‘Taonani! Mofanana ndi chiwombankhanga chimene chimatsika nʼkugwira chakudya chake,+
Mdani adzatambasula mapiko ake nʼkugwira Mowabu.+
41 Matauni adzalandidwa,
Ndipo malo ake otetezeka adzalandidwa.
Pa tsiku limenelo, mitima ya asilikali a ku Mowabu
Idzakhala ngati mtima wa mkazi amene akubereka.
42 Mowabu adzawonongedwa ndipo sadzakhalanso mtundu wa anthu,+
Chifukwa wadzikweza pamaso pa Yehova.+
43 Mantha, dzenje ndi msampha zili pa iwe,
Iwe munthu wokhala ku Mowabu,’ akutero Yehova.
44 ‘Aliyense amene akuthawa chifukwa cha mantha adzagwera mʼdzenje,
Ndipo aliyense amene akutuluka mʼdzenjemo adzagwidwa mumsampha.
Chifukwa ndidzapereka chilango kwa anthu a ku Mowabu mʼchaka chimene ndasankha,’ akutero Yehova.
45 ‘Anthu amene akuthawa aima mumthunzi wa Hesiboni ndipo alibe mphamvu.
Chifukwa moto udzachokera ku Hesiboni
Ndipo malawi a moto adzachokera ku Sihoni.+
Motowo udzawotcha Mowabu pachipumi
Komanso mitu ya ana achiwawa.+
46 Tsoka iwe Mowabu!
Anthu a Kemosi+ awonongedwa.
Ana ako aamuna agwidwa ndi adani,
Ndipo ana ako aakazi atengedwa kupita kudziko lina.+
47 Koma mʼmasiku otsiriza ine ndidzasonkhanitsa Amowabu onse amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,’ akutero Yehova.
‘Apa ndi pamene pathera chiweruzo chokhudza Mowabu.’”+