Luka
13 Pa nthawiyo, panali anthu ena amene anam’fotokozera za Agalileya+ amene magazi awo, Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo. 2 Choncho poyankha iye anawauza kuti: “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewo anali ochimwa kwambiri+ kuposa Agalileya ena onse chifukwa chakuti zimenezo zinawachitikira? 3 Ndithudi ayi. Choncho ndikukuuzani kuti ngati simulapa, nonsenu mudzawonongeka mofanana ndi iwowo.+ 4 Nanga bwanji za anthu 18 aja, amene nsanja inawagwera ku Siloamu n’kuwapha? Kodi mukuganiza kuti iwo anali ochimwa kwambiri kuposa anthu onse okhala mu Yerusalemu? 5 Ndithudi ayi. Choncho ndikukuuzani kuti, ngati simulapa, nonsenu mudzawonongeka ngati mmene iwo anawonongekera.”+
6 Kenako anayamba kufotokoza fanizo ili: “Munthu wina anali ndi mkuyu m’munda wake wa mpesa,+ ndipo anapita kukafuna chipatso mumtengowo,+ koma sanapezemo chilichonse.+ 7 Ndiyeno anauza munthu wosamalira munda wa mpesawo kuti, ‘Kwa zaka zitatu+ tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna nkhuyu mumtengo uwu, koma sindinapezemo ngakhale imodzi. Dula mtengo umenewu!+ N’chifukwa chiyani ukungowononga nthaka?’ 8 Wosamalira mundayo anayankha kuti, ‘Mbuyanga, bwanji muusiye+ chaka chino chokha. Ine ndikumba mouzungulira n’kuthirapo manyowa. 9 Ukadzabala zipatso m’tsogolo, zidzakhala bwino, koma ngati sudzabala mudzaudule.’”+
10 Tsopano anali kuphunzitsa m’sunagoge winawake pa sabata. 11 Mmenemo munali mayi wina amene mzimu+ woipa unamudwalitsa zaka 18. Anali wopindika msana moti sankatha kuweramuka. 12 Yesu atamuona, anamulankhula kuti: “Mayi, mwamasuka+ ku matenda anu.” 13 Pamenepo anaika manja ake pamayiyo, ndipo nthawi yomweyo anaweramuka,+ n’kuyamba kutamanda Mulungu. 14 Koma mtsogoleri wa sunagoge ataona izi, anakwiya chifukwa Yesu anachiritsa munthu pa sabata.+ Choncho anayamba kuuza khamu la anthu kuti: “Pali masiku 6 oyenera kugwira ntchito. Muzibwera masiku amenewo kudzachiritsidwa, osati tsiku la sabata.”+ 15 Koma Ambuye anamuyankha kuti: “Onyenga inu,+ kodi aliyense wa inu samasula ng’ombe yake kapena bulu wake m’khola pa sabata ndi kupita naye kukam’mwetsa madzi?+ 16 Kodi sikunali koyenera kuti mayi uyu, amenenso ndi mwana wa Abulahamu,+ amene Satana anamumanga zaka 18, amasulidwe m’maunyolo amenewa tsiku la sabata?” 17 Atanena zimenezi, onse omutsutsa anachita manyazi.+ Koma khamu lonse la anthu linayamba kukondwera ndi zodabwitsa zonse zimene iye anachita.+
18 Pamenepo anapitiriza kuti: “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani, ndiuyerekeze ndi chiyani?+ 19 Uli ngati kanjere ka mpiru,* kamene munthu anakatenga ndi kukaponya m’munda wake. Kenako kanamera ndi kukhala mtengo, moti mbalame zam’mlengalenga+ zinapeza malo okhala m’nthambi zake.”+
20 Iye ananenanso kuti: “Kodi ufumu wa Mulungu ndiuyerekeze ndi chiyani? 21 Uli ngati chofufumitsa chimene mayi wina anachitenga ndi kuchibisa mu ufa wokwana mbale zoyezera zazikulu zitatu, moti mtanda wonsewo unafufuma.”+
22 Yesu anayenda mumzinda ndi mzinda, komanso mudzi ndi mudzi. Anali kuphunzitsa ndi kupitiriza ulendo wake wopita ku Yerusalemu.+ 23 Tsopano munthu wina anamufunsa kuti: “Ambuye, kodi amene akupulumuka ndi owerengeka okha?”+ Iye anawauza kuti: 24 “Yesetsani+ mwamphamvu kulowa pakhomo lopapatiza.+ Chifukwa ambiri ndikukuuzani, adzafunitsitsa kulowamo koma sadzatha.+ 25 Mwininyumba akanyamuka ndi kukakhoma chitseko, ndiyeno inu n’kuima panja ndi kuyamba kugogoda pachitsekopo, n’kumanena kuti, ‘Titsegulireni ambuye,’+ iye poyankha adzakuuzani kuti, ‘Sindikudziwa kumene mukuchokera.’+ 26 Pamenepo mudzayamba kunena kuti, ‘Tinadya ndi kumwa pamaso panu, ndipo inu munaphunzitsa m’misewu yathu.’+ 27 Koma iye adzakuuzani kuti, ‘Sindikudziwa kumene mukuchokera. Ndichokereni pano, nonsenu ochita zinthu zosalungama!’+ 28 Kunjako n’kumene inu mudzalira ndi kukukuta mano,+ pamene mudzaona Abulahamu, Isaki ndi Yakobo, komanso aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu,+ koma inuyo atakukankhirani kunja. 29 Komanso, anthu adzabwera kuchokera kumbali za kum’mawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kum’mwera,+ ndipo adzadya patebulo mu ufumu wa Mulungu.+ 30 Ndithudi amene ali omalizira adzakhala oyamba, ndipo oyamba adzakhala omalizira.”+
31 Mu ola lomwelo kunafika Afarisi ena ndi kumuuza kuti: “Nyamukani muchoke kuno, chifukwa Herode* akufuna kukuphani.” 32 Iye anawayankha kuti: “Pitani mukaiuze nkhandwe+ imeneyo kuti, ‘Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchita ntchito yochiritsa lero ndi mawa, tsiku lachitatu ndidzamaliza.’+ 33 Komabe ndiyenera kupitiriza ulendo wanga lero ndi mawa ndi tsiku linalo, chifukwa n’kosayenera kuti mneneri amuphere kunja kwa Yerusalemu.+ 34 Yerusalemu, Yerusalemu! wakupha+ aneneri ndi kuponya miyala+ anthu otumidwa kwa iwe . . . mobwerezabwereza ndinafuna kusonkhanitsa ana ako monga mmene nkhuku yathadzi imasonkhanitsira anapiye ake m’mapiko ake,+ koma anthu inu simunafune zimenezo.+ 35 Tsopano tamverani! Mulungu wachoka ndi kukusiyirani nyumba* yanuyi.+ Ndithu ndikukuuzani, simudzandionanso kufikira pamene mudzanene kuti, ‘Wodalitsidwa iye wobwera m’dzina la Yehova!’”+