Numeri
23 Tsopano Balamu anauza Balaki kuti: “Mundimangire pamalo ano maguwa ansembe+ okwanira 7. Mukatero mundikonzere ng’ombe zamphongo 7, ndi nkhosa zamphongo 7.” 2 Nthawi yomweyo Balaki anachita monga momwe anamuuzira Balamu. Kenako, Balaki ndi Balamu anapereka nsembe. Anapereka ng’ombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo paguwa lililonse.+ 3 Ndiyeno Balamu anauza Balaki kuti: “Muime pafupi ndi nsembe yanu yopsereza.+ Mundilole ine ndichoke, kuti mwina Yehova akumana nane n’kundilankhula.+ Akatero, zimene andiuzezo n’zimenenso ndinene kwa inu.” Chotero Balamu anapita pamwamba pa phiri.
4 Mulungu atam’peza Balamu,+ iye anamuuza Mulunguyo kuti: “Ndamanga maguwa ansembe 7 m’mizere, ndipo ndapereka nsembe ng’ombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo paguwa lililonse.”+ 5 Pamenepo Yehova anamuika Balamu+ mawu m’kamwa, n’kumuuza kuti: “Bwerera kwa Balaki, ukamuuze mawu amenewa.”+ 6 Iye atabwerera kwa Balaki, anapeza Balakiyo limodzi ndi akalonga onse a ku Mowabu ataima pafupi ndi nsembe yake yopsereza. 7 Pamenepo Balamu anayamba kulankhula mwa ndakatulo,+ kuti:
“Balaki mfumu ya Mowabu yandiitana kuchokera ku Aramu,+
Kuchokera kumapiri a kum’mawa, kuti:
‘Bwera, udzanditembererere Yakobo.
Bwera, udzaitanire tsoka pa Isiraeli.’+
8 Ndingathe bwanji kutemberera anthu amene Mulungu sanawatemberere?+
Anthu amene Yehova sanawaitanire tsoka, ndingathe bwanji kuwaitanira tsoka?+
9 Pakuti pomwe ndili pano ndikutha kuwaona, pamwamba pa matanthwe pano,
Ndikuwaona ndithu, pano pamwamba pa mapiri.
Akukhala paokhaokha m’mahema awo,+
Iwo akudziona kuti ndi osiyana ndi mitundu ina.+
10 Ndani watha kuwerenga mtundu wa Yakobo,+ wochuluka ngati fumbi,
Ndipo ndani watha kuwerenga gawo limodzi mwa magawo anayi a Isiraeli?
Moyo wanga ufe imfa ya olungama,+
Ndipo mathero anga akhale ngati awo.”+
11 Balaki atamva zimenezi anafunsa Balamu kuti: “N’chiyani mwandichitachi? Ndinakutengani kuti mudzatemberere adani anga, koma inu mwawadalitsa kwambiri.”+ 12 Koma iye anamuyankha kuti: “Kodi chilichonse chimene Yehova wandiika m’kamwa, si chimene ndinayenera kunena?”+
13 Ndiyeno Balaki anauza Balamu kuti: “Tabwerani chonde, tiyeni tipite kumalo ena kumene mungathe kuwaona anthuwo. Simukaona onse, koma mukangoona okhawo amene ali chakufupi.+ Mukanditembererere amenewo.”+ 14 Chotero anamutengera ku Zofimu, pamwamba pa phiri la Pisiga.+ Kumeneko anamanga maguwa ansembe 7, n’kupereka nsembe ng’ombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo paguwa lililonse.+ 15 Pambuyo pake, Balamu anauza Balaki kuti: “Muime pano, pafupi ndi nsembe yanu yopserezayi koma ine mundilole ndichoke ndikalankhule ndi Mulungu uko.” 16 Kumeneko Yehova analankhuladi ndi Balamu, n’kumuika mawu m’kamwa, ndipo anamuuza kuti:+ “Bwerera kwa Balaki+ ukamuuze zimenezi.” 17 Balamu atabwerera kwa Balaki, anam’peza ataima pafupi ndi nsembe yake yopsereza, akalonga a ku Mowabu ali naye limodzi pamenepo. Ndiyeno Balaki anafunsa Balamu kuti: “Kodi Yehova wati chiyani?” 18 Pamenepo Balamu anayambanso kulankhula mwa ndakatulo, kuti:+
“Nyamuka, Balaki iwe, tamvera.
Tchera khutu kwa ine, iwe mwana wa Zipori.+
19 Mulungu si munthu, woti anganene mabodza,+
Si mwana wa munthu, woti angadzimve kuti ali ndi mlandu.+
Kodi ananenapo kanthu koma osachita,
Analankhulapo kanthu kodi koma osakwaniritsa?+
21 Iye sanaone mphamvu yamatsenga+ iliyonse ikuchita kanthu pa Yakobo,
Ndipo sanaone Isiraeli akuponyeredwa vuto.
Mulungu wake Yehova ali naye,+
Ndipo mfuu yotamanda mfumu ikumveka pakati pake.
23 Palibe amene walodza Yakobo,+
Ngakhale kuchesa Isiraeli.+
Za Yakobo ndi Isiraeli, adzati,
‘Mwaonatu zimene Mulungu wachita!’+
24 Taonani, mtundu udzadzuka ngati mkango,
Udzanyamuka monga mkango.+
Sugona pansi mpaka ugwire nyama,
Ndipo udzamwa magazi a ophedwawo.”+
25 Tsopano Balaki anauza Balamu kuti: “Ngati mwalephera kuwatemberera ngakhale pang’ono pokha, ndiye musawadalitsenso m’pang’ono pomwe.” 26 Pamenepo Balamu anafunsa Balaki kuti: “Kodi sindinanene kwa inu kuti, ‘Ndichita zokhazo zimene Yehova andiuze’?”+
27 Koma Balaki anauza Balamu kuti: “Chonde tabwerani. Tiyeni tipite kumalo enanso. Mwina kumeneko Mulungu woona angalole kuti munditembererere anthuwa.”+ 28 Balaki atatero, anatengera Balamu pamwamba pa phiri la Peori, loyang’ana ku Yesimoni.+ 29 Kumeneko Balamu+ anauza Balaki kuti: “Mundimangire pamalo ano maguwa ansembe 7, ndipo mundikonzere ng’ombe zamphongo 7, ndi nkhosa zamphongo 7.”+ 30 Chotero Balaki anachita monga momwe Balamu ananenera. Anapereka nsembe ng’ombe yamphongo ndi nkhosa yamphongo paguwa lililonse.+