Luka
23 Pamenepo khamu lonselo linanyamuka, onse pamodzi, n’kupita naye kwa Pilato.+ 2 Ndiyeno anayamba kumuneneza+ kuti: “Ife tapeza munthu uyu akupandutsa+ mtundu wathu ndi kuletsa anthu kuti asamakhome msonkho+ kwa Kaisara, komanso iyeyu akunena kuti ndi Khristu mfumu.”+ 3 Tsopano Pilato anamufunsa funso kuti: “Kodi ndiwe mfumu ya Ayuda?” Pomuyankha iye anati: “Mukunena nokha.”+ 4 Pamenepo Pilato anauza ansembe aakulu ndi khamu la anthulo kuti: “Sindikupeza mlandu uliwonse mwa munthu uyu.”+ 5 Koma iwo anaumirira kuti: “Iyeyu akusokoneza anthu mwa kuphunzitsa mu Yudeya monse, ngakhalenso kuyambira ku Galileya mpaka kudzafika kuno.” 6 Atamva zimenezo, Pilato anafunsa ngati munthuyu ndi Mgalileya. 7 Ndiyeno, atadziwa kuti ndi wochokera m’chigawo cholamulidwa ndi Herode,*+ anamutumiza kwa Herode, amene m’masiku amenewo anali mu Yerusalemu.
8 Herode ataona Yesu anakondwera kwambiri, chifukwa kwa nthawi yaitali ndithu anali kufunitsitsa kuti amuone+ popeza anali kumva+ za iye. Komanso anali kuyembekezera kuona chizindikiro chimene iye angachite. 9 Tsopano anayamba kumufunsa zambiri, koma iye sanayankhe.+ 10 Komabe ansembe aakulu ndi alembi anali kumangonyamukanyamuka ndi kumuneneza mwaukali.+ 11 Pamenepo Herode pamodzi ndi asilikali ake omulondera anamupeputsa.+ Anamuchitira zachipongwe+ mwa kumuveka chovala chonyezimira ndipo anamutumizanso kwa Pilato. 12 Tsiku lomwelo Herode ndi Pilato+ anakhala mabwenzi tsopano, koma m’mbuyo monsemo izi zisanachitike, anali pa udani.
13 Ndiyeno Pilato anasonkhanitsa ansembe aakulu, olamulira ndi anthu ena 14 ndi kuwauza kuti: “Inu mwabweretsa munthu uyu kwa ine monga wolimbikitsa anthu kuukira. Koma mwaona nokha pano! Inetu ndamufunsa pamaso panu, ndipo sindinamupeze ndi chifukwa+ chomuimbira milandu imene mukumunenezayi. 15 Ndipotu ngakhale Herode sanam’peze ndi mlandu, n’chifukwa chake wam’bweza kwa ife. Ndithudi ameneyu sanachite chilichonse choyenera chilango cha imfa.+ 16 Choncho ndingomukwapula+ ndi kumumasula.” 17* —— 18 Koma khamu lonse linafuulira pamodzi kuti: “Ameneyu muthane naye basi,+ koma ife mutimasulire Baraba!”+ 19 (Munthu ameneyu anaponyedwa m’ndende chifukwa cha kuukira boma kumene kunachitika mumzindawo, komanso chifukwa chopha munthu.) 20 Pilato analankhula nawo kachiwiri, chifukwa anali wofunitsitsa kumasula Yesu.+ 21 Pamenepo anthuwo anayamba kufuula kuti: “M’pachikeni! M’pachikeni!”+ 22 Anawafunsa kachitatu kuti: “Chifukwa chiyani? Kodi iyeyu walakwa chiyani? Ine sindikumupeza ndi chifukwa chilichonse chomuphera, choncho ndimukwapula ndi kumumasula.”+ 23 Atamva izi, anayamba kumuumiriza mokweza mawu, ndi kumupempha kuti Yesu apachikidwe basi. Anthuwo anali kufuula mwamphamvu moti Pilato anangololera.+ 24 Choncho Pilato anapereka chiweruzo chokwaniritsa zofuna za anthuwo.+ 25 Iye anamasula+ munthu woponyedwa m’ndende pa mlandu woukira boma ndi kupha munthu, amenenso anthuwo anapempha kuti amumasule. Koma Yesu anamupereka m’manja mwawo kuti zofuna zawo zichitike.+
26 Pamene anali kupita naye, iwo anagwira Simoni, nzika ya ku Kurene, amene anali kuchokera kudera lakumidzi. Iwo anamusenzetsa mtengo wozunzikirapo,* kuti aunyamule ndi kumatsatira pambuyo pa Yesu.+ 27 Koma khamu lalikulu la anthu linali kumutsatira pamodzi ndi amayi ambiri amene anali kudziguguda pachifuwa chifukwa cha chisoni ndipo anali kumulirira. 28 Yesu anacheukira amayiwo ndi kunena kuti: “Ana aakazi a Yerusalemu inu, lekani kundilirira. Koma mudzilirire nokha ndi ana anu.+ 29 Chifukwa masiku akubwera pamene anthu adzanena kuti, ‘Odala ndi akazi osabereka, amene sanaberekepo, komanso amene mabere awo sanayamwitsepo!’+ 30 M’masiku amenewo iwo adzayamba kuuza mapiri kuti, ‘Tigwereni!’ ndipo adzauza zitunda kuti, ‘Tikwirireni!’+ 31 Pakuti ngati akuchita izi pamene mtengo uli wauwisi, kuli bwanji mtengowo ukadzauma?”+
32 Anthuwo anatenganso amuna ena awiri ochita zoipa, kuti akawaphe limodzi ndi Yesu.+ 33 Tsopano atafika pamalo otchedwa Chibade,+ anamupachika pamenepo pamodzi ndi amuna ochita zoipawo. Mmodzi anamupachika kudzanja lake lamanja, wina kumanzere kwake.+ 34 [[Koma Yesu anati: “Atate, akhululukireni,+ chifukwa sakudziwa chimene akuchita.”]]* Ndipo iwo anagawana malaya ake mwa kuchita maere.+ 35 Anthu anangoima chilili kuonerera zochitikazo.+ Koma olamulira anali kumunyogodola kuti: “Ena anatha kuwapulumutsa, m’lekeni adzipulumutse yekha,+ ngati iyeyu alidi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwa.”+ 36 Asilikali nawonso anamuchitira zachipongwe,+ anamuyandikira ndi kumupatsa vinyo wowawasa+ 37 ndi kunena kuti: “Ngati ulidi mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.” 38 Pamwamba pake analembapo mawu akuti: “Uyu ndiye mfumu ya Ayuda.”+
39 Komanso mmodzi wa ochita zoipa amene anapachikidwa naye pamodziwo anayamba kumulankhulira zachipongwe+ kuti: “Kodi si iwe Khristu? Dzipulumutse wekha, limodzi ndi ife.” 40 Poyankha mnzake uja anamudzudzula kuti: “Kodi iwe suopa Mulungu eti, poona kuti nawenso ukulandira chilango chofanana ndi cha munthu ameneyu?+ 41 Ifetu m’pake kulangidwa chonchi, pakuti tikulandiriratu zonse zotiyenera malinga ndi zimene tinachita. Koma munthu uyu sanalakwe chilichonse.”+ 42 Kenako anapitiriza kunena kuti: “Yesu, mukandikumbukire mukakalowa mu ufumu wanu.”+ 43 Pamenepo Yesu anamuuza kuti: “Ndithu ndikukuuza lero, Iwe udzakhala ndi ine+ m’Paradaiso.”+
44 Tsopano nthawi inali cha m’ma 12 koloko masana,* koma kunagwa mdima padziko lonse lapansi mpaka 3 koloko masana,*+ 45 popeza dzuwa linachita mdima. Pa nthawi imeneyi nsalu yotchinga+ ya m’nyumba yopatulika inang’ambika pakati+ kuchokera pamwamba mpaka pansi. 46 Pamenepo Yesu anafuula mokweza mawu kuti: “Atate, ndikuikiza mzimu*+ wanga m’manja mwanu.” Atanena zimenezi anatsirizika.+ 47 Poona zochitikazo, kapitawo wa asilikali anayamba kutamanda Mulungu kuti: “Ndithudi munthu uyu anali wolungama.”+ 48 Anthu onse amene anasonkhana kumeneko kudzaona zochitikazo, ataona zonse zimene zinachitika, anayamba kubwerera akudziguguda pachifuwa. 49 Komanso onse amene anali kumudziwa anaimirira chapatali ndithu.+ Ndipo amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anaimiriranso chapomwepo n’kumaonerera zinthu zimenezi.+
50 Tsopano panali mwamuna wina dzina lake Yosefe, amene anali wa m’Khoti Lalikulu la Ayuda, munthu wabwino ndi wolungama.+ 51 Munthu ameneyu sanavomereze chiwembu chawo ndi zochita zawo.+ Yosefe anali wochokera ku Arimateya, mzinda wa Ayudeya, ndipo anali kuyembekezera ufumu wa Mulungu.+ 52 Iye anapita kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu.+ 53 Choncho anautsitsa+ ndi kuukulunga munsalu yabwino kwambiri, kenako anakauika m’manda+ ogobedwa muthanthwe, mmene anali asanaikemo munthu chikhalire.+ 54 Tsopano linali Tsiku Lokonzekera,+ ndipo chisisira cha madzulo chosonyeza kuyambika kwa sabata+ chinali kuyambika. 55 Koma amayi amene anayenda limodzi ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anamutsatira kukaona manda achikumbutsowo+ ndi mmene mtembo wakewo anauikira.+ 56 Atatero anabwerera kukakonza zonunkhiritsa ndi mafuta onunkhira.+ Komabe pa tsiku la sabata+ anapuma malinga ndi chilamulo.