Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 22:kam-31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe motsatira Mbawala Yaikazi ya M’bandakucha. Nyimbo ya Davide.

      22 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?+

      N’chifukwa chiyani mukuchedwa kundipulumutsa?+

      N’chifukwa chiyani simukumva mawu a kubuula kwanga?+

       2 Inu Mulungu wanga, ine ndimaitana usana koma simundiyankha.+

      Usiku ndimaitanabe, moti sindikukhala chete.+

       3 Koma inu ndinu woyera.+

      Mukukhala pakati pa zitamando za Isiraeli.+

       4 Makolo athu anali kudalira inu.+

      Iwo anali kudalira inu ndipo munali kuwapulumutsa.+

       5 Iwo anali kufuulira inu,+ ndipo anali kupulumuka.+

      Anali kudalira inu, ndipo simunawachititse manyazi.+

       6 Koma ine ndine nyongolotsi+ osati munthu.

      Anthu amanditonza ndipo ndine wonyozeka kwa anthu.+

       7 Anthu onse ondiona amandinyodola.+

      Iwo amandinyogodola ndi pakamwa pawo, ndipo amapukusa mitu yawo mondinyoza.+ Iwo amati:

       8 “Anadzipereka kwa Yehova.+ Amupulumutse Iyeyo!+

      Ngati Mulungu amamukonda, amulanditse!”+

       9 Pakuti ndinu amene munanditulutsa m’mimba,+

      Amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinali kuyamwa mabere a mayi anga.+

      10 Ndinaponyedwa m’manja mwanu kuchokera m’mimba.+

      Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga, inu mwakhala Mulungu wanga.+

      11 Musakhale kutali ndi ine, chifukwa zondisautsa zili pafupi,+

      Ndiponso chifukwa ndilibe mthandizi winanso.+

      12 Ng’ombe zazing’ono zamphongo zochuluka zandizungulira.+

      Nkhunzi zamphamvu za ku Basana zandizinga.+

      13 Iwo anditsegulira pakamwa pawo mondiopseza,+

      Ngati mkango wokhadzula nyama umenenso ukubangula.+

      14 Ndathiridwa pansi ngati madzi.+

      Mafupa anga onse alekanalekana.+

      Mtima wanga wakhala ngati phula,+

      Wasungunuka mkati mwanga.+

      15 Mphamvu yanga yauma gwaa, ngati phale.+

      Lilime langa lamamatira kunkhama zanga,+

      Ndipo mwandikhazika m’fumbi la imfa.+

      16 Agalu andizungulira.+

      Khamu la anthu ochita zoipa landizinga.+

      Iwo akuluma manja ndi mapazi anga ngati mkango.+

      17 Ndingathe kuwerenga mafupa anga onse.+

      Adaniwo akuona zimenezi, ndipo akundiyang’anitsitsa.+

      18 Iwo akugawana zovala zanga pakati pawo,+

      Ndipo akuchita maere pazovala zanga.+

      19 Koma inu Yehova, musakhale kutali ndi ine,+

      Inu mphamvu yanga,+ ndithandizeni mofulumira.+

      20 Landitsani moyo wanga ku lupanga,+

      Moyo wanga wokhawu umene ndili nawo muulanditse m’kamwa mwa galu.+

      21 Ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango,+

      Ndipo mundiyankhe ndi kundipulumutsa ku nyanga za ng’ombe zamphongo zam’tchire.+

      22 Ndidzalengeza dzina lanu+ kwa abale anga.+

      Ndidzakutamandani pakati pa mpingo.+

      23 Inu oopa Yehova, m’tamandeni!+

      Inu nonse mbewu ya Yakobo, m’patseni ulemerero!+

      Ndipo muopeni, inu nonse mbewu ya Isiraeli.+

      24 Pakuti iye sananyoze,+

      Kapena kunyansidwa ndi nsautso ya munthu wosautsidwa.+

      Ndipo sanam’bisire nkhope yake.+

      Pamene anamulirira kuti amuthandize, iye anamva.+

      25 Chifukwa cha zimene mwachita ndidzakutamandani mumpingo waukulu.+

      Ndidzakwaniritsa malonjezo anga pamaso pa anthu oopa iye.+

      26 Ofatsa adzadya ndi kukhuta.+

      Ofunafuna Yehova adzamutamanda.+

      Mitima yanu ikhale ndi moyo kosatha.+

      27 Anthu onse okhala kumalekezero a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kubwerera kwa iye.+

      Ndipo mafuko onse a anthu a mitundu ina adzagwada pamaso panu.+

      28 Pakuti Yehova ndiye mfumu,+

      Ndipo akulamulira mitundu.+

      29 Anthu onse a padziko lapansi onyada chifukwa cha chuma chawo adzadya ndi kuwerama.+

      Onse otsikira kufumbi adzawerama pamaso pake,+

      Ndipo palibe amene adzapulumutsa moyo wake.+

      30 Mbewu idzamutumikira.+

      Adzalengeza za Yehova ku m’badwo wotsatira.+

      31 Adzafika ndi kunena za chilungamo chake,+

      Adzauza anthu amene adzabadwe kuti iye ndiye wachita zimenezi.+

  • Yesaya 53:1-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 53 Kodi ndani wakhulupirira zimene ife tamva?+ Ndipo kodi dzanja la Yehova+ laonetsedwa kwa ndani?+ 2 Iye adzaphuka ngati nthambi+ pamaso pa winawake, ndiponso ngati muzu m’dziko lopanda madzi. Alibe maonekedwe alionse apamwamba kapena okongola,+ ndipo maonekedwe ake si osiririka m’maso mwathu.+

      3 Iye ananyozedwa ndipo anthu anali kumupewa.+ Anali munthu amene anadziwa kupweteka ndiponso amene anadziwa matenda.+ Ife tinali kuyang’ana kumbali kuti tisaone nkhope yake.+ Ananyozedwa ndipo tinamuona ngati wopanda pake.+ 4 Zoonadi, iye anatinyamulira matenda athu+ ndipo anatisenzera zowawa zathu.+ Koma ifeyo tinamuona ngati wosautsidwa,+ wokwapulidwa ndi Mulungu,+ ndiponso wozunzidwa.+ 5 Iye anabayidwa+ chifukwa cha zolakwa zathu.+ Anaphwanyidwa chifukwa cha zochimwa zathu.+ Chilango chotibweretsera mtendere chinam’gwera iyeyo,+ ndipo chifukwa cha zilonda zake+ ifeyo tachiritsidwa.+ 6 Tonsefe tinkangoyendayenda uku ndi uku ngati nkhosa.+ Aliyense analowera njira yake ndipo Yehova wachititsa cholakwa cha aliyense wa ife kugwera pa ameneyo.+ 7 Iye anapanikizidwa+ ndipo analola kuti asautsidwe,+ koma sanatsegule pakamwa pake. Anatengedwa ngati nkhosa yopita kokaphedwa,+ ndipo mofanana ndi nkhosa yaikazi imene imakhala chete akamaimeta ubweya, nayenso sanatsegule pakamwa pake.+

      8 Iye anaponderezedwa ndipo anatengedwa popanda kuweruzidwa mwachilungamo.+ Ndani amene anaganizira tsatanetsatane wa mibadwo ya makolo ake?+ Pakuti iye anadulidwa+ m’dziko la amoyo.+ Chifukwa cha zolakwa+ za anthu anga, iye anakwapulidwa.+ 9 Manda ake adzakhala limodzi ndi a anthu oipa,+ ndipo adzakhala limodzi ndi anthu olemera pa imfa yake,+ ngakhale kuti iye sanachite zachiwawa zilizonse+ ndipo m’kamwa mwake munalibe chinyengo.+

      10 Koma zinamukomera Yehova kuti mtumiki wake aphwanyidwe.+ Iye anamulola kuti adwale.+ Mukapereka moyo wake monga nsembe ya kupalamula,+ iye adzaona ana ake.+ Adzatalikitsa masiku ake+ ndipo ndi dzanja lake, adzakwaniritsa zokonda+ Yehova.+ 11 Chifukwa cha kuvutika kwake, iye adzaona zabwino+ ndipo adzakhutira.+ Chifukwa cha zimene akudziwa, mtumiki wanga wolungamayo+ adzachititsa kuti anthu ambiri azionedwa olungama,+ ndipo adzasenza zolakwa zawo.+ 12 Pa chifukwa chimenechi, ndidzamupatsa gawo pamodzi ndi ambiri+ ndipo iye adzagawana zolanda ndi amphamvu,+ chifukwa anakhuthula moyo wake mu imfa+ ndipo anaonedwa monga mmodzi wa ochimwa.+ Iye ananyamula tchimo la anthu ambiri+ ndipo analowererapo kuti athandize olakwa.+

  • Yohane 20:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Kenako anauza Tomasi kuti: “Ika chala chako apa, ndiponso ona m’manja mwangamu. Gwiranso ndi dzanja lako+ m’mbali mwa mimba yangamu, kuti usakhalenso wosakhulupirira, koma wokhulupirira.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena