Machitidwe
21 Tsopano titadzikakamiza kulekana nawo n’kuyamba ulendo wathu wa panyanja, tinayenda molunjika mpaka kufika ku Ko. Koma tsiku lotsatira tinafika ku Rode, ndipo titachoka kumeneko tinakafika ku Patara. 2 Kumeneko tinapeza ngalawa imene inali kuwolokera ku Foinike, ndipo tinakwera ndi kunyamuka. 3 Chilumba cha Kupuro+ chitayamba kuonekera, tinachisiya kumanzere ndi kupitiriza ulendo wathu kulowera ku Siriya.+ Tinaima ku Turo, chifukwa kumeneko ngalawa inafunika kutsitsa katundu.+ 4 Titafufuza tinapeza ophunzira ndi kukhala nawo kumeneko masiku 7. Koma mouziridwa ndi mzimu,+ iwo anauza Paulo mobwerezabwereza kuti asakaponde mu Yerusalemu. 5 Choncho titatsiriza masikuwo, tinanyamuka kuti tipitirize ulendo wathu. Ndipo abale onse, pamodzi ndi amayi ndi ana, anatiperekeza mpaka kunja kwa mzindawo. Kumeneko tinagwada+ pagombe ndi kupemphera 6 n’kutsanzikana.+ Kenako ife tinakwera ngalawa ndipo iwo anabwerera kunyumba zawo.
7 Choncho tinanyamuka ku Turo pangalawa ndipo tinafika ku Tolemayi. Kumeneko tinalonjerana ndi abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi. 8 M’mawa mwake tinanyamuka ndi kukafika ku Kaisareya.+ Kumeneko tinakalowa m’nyumba ya mlaliki* Filipo. Iyeyu anali mmodzi wa amuna 7 a mbiri yabwino aja,+ ndipo tinakhala naye. 9 Mwamuna ameneyu anali ndi ana aakazi anayi, anamwali, amene anali kunenera.+ 10 Koma titakhala masiku ndithu, mneneri wina dzina lake Agabo+ anafika kumeneko kuchokera ku Yudeya. 11 Iye anafika kwa ife ndi kutenga lamba wa Paulo. Kenako anadzimanga mapazi ndi manja ndi kunena kuti: “Mzimu woyera wati, ‘Mwiniwake wa lambayu, Ayuda adzamumanga+ chonchi ku Yerusalemu ndi kumupereka+ m’manja mwa anthu a mitundu ina.’” 12 Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu akumeneko, tinayamba kuchonderera Paulo kuti asapite+ ku Yerusalemu. 13 Koma Paulo anayankha kuti: “N’chifukwa chiyani mukulira+ ndi kunditayitsa mtima?+ Dziwani kuti ine ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha, komanso kukafa+ ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.” 14 Titalephera kumusintha maganizo, tinangovomereza ndi kunena kuti: “Chifuniro+ cha Yehova chichitike.”
15 Masiku amenewa atapita, tinakonzekera ulendo ndipo tinanyamuka kulowera ku Yerusalemu.+ 16 Koma ophunzira ena a ku Kaisareya+ ananyamuka nafe, kuti atiperekeze kunyumba ya munthu wina kuti tikafikire kumeneko. Munthu ameneyu dzina lake linali Mnaso wa ku Kupuro, ndipo anali mmodzi wa ophunzira oyambirira. 17 Titafika ku Yerusalemu,+ abale anatilandira mokondwa.+ 18 Koma tsiku lotsatira, Paulo anapita nafe kwa Yakobo,+ ndipo akulu onse anali komweko. 19 Paulo anawalonjera ndi kuyamba kuwafotokozera mwatsatanetsatane+ zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.+
20 Iwo atamva zimenezi anayamba kutamanda Mulungu, ndipo anamuuza kuti: “M’bale, kodi ukuona kuchuluka kwa okhulupirira amene ali pakati pa Ayuda? Ndipo onsewa ndi odzipereka pa nkhani yotsatira Chilamulo.+ 21 Komatu iwo amva mphekesera zakuti iwe wakhala ukuphunzitsa Ayuda onse amene ali pakati pa anthu a mitundu ina kuti apandukire Chilamulo cha Mose.+ Akuti ukuwauza kuti asamachite mdulidwe+ wa ana awo kapena kutsatira miyambo imene takhala tikuitsatira kuyambira kale. 22 Tsopano tichite chiyani pamenepa? Sitikukayikira kuti iwo adzamva ndithu kuti iwe wafika. 23 Choncho uchite zimene tikuuze pano: Tili ndi amuna anayi amene anachita lumbiro. 24 Utenge amuna amenewa+ ndipo ukachite mwambo wa kudziyeretsa pamodzi ndi iwo. Uwalipirire zonse zofunika,+ kuti amete tsitsi lawo.+ Ukatero, aliyense adzadziwa kuti mphekesera zimene anamva za iwe ndi nkhambakamwa chabe. Adzaona kuti ukuchita zinthu motsatira dongosolo, komanso kuti umasunga Chilamulo.+ 25 Koma kwa okhulupirira ochokera mwa anthu a mitundu inawo, tinawatumizira chigamulo chathu chakuti apewe zoperekedwa nsembe kwa mafano+ komanso magazi,+ zopotola,+ ndi dama.”+
26 Choncho Paulo anatenga amunawo tsiku lotsatira ndi kukachita mwambo wa kudziyeretsa pamodzi ndi iwo.+ Kenako analowa m’kachisi, kukanena pamene masiku awo a mwambo wa kudziyeretsa adzathere,+ ndi pamene aliyense wa iwo adzamuperekere nsembe.+
27 Ali pafupi kutsiriza masiku 7,+ Ayuda ochokera ku Asia anaona Paulo ali m’kachisi. Chotero anayambitsa chisokonezo+ m’khamu lonse la anthu ndipo anamugwira. 28 Iwo anali kufuula kuti: “Inu Aisiraeli, tithandizeni! Munthu amene akuphunzitsa zotsutsana ndi anthu a mtundu wathu kulikonse ndi ameneyu.+ Iyeyu akuphunzitsa zotsutsana ndi Chilamulo komanso malo ano. Kuwonjezera pamenepo, inu mukudziwa kuti anatenga Agiriki n’kudzawalowetsa m’kachisi ndipo waipitsa malo oyera ano.”+ 29 Iwo ananena zimenezi chifukwa tsiku lina anaona Terofimo+ wa ku Efeso ali naye limodzi mumzindawo. Atawaona anaganiza kuti Paulo analowetsa Terofimo m’kachisi. 30 Chotero munali chisokonezo mumzinda wonsewo, ndipo anthu anali balalabalala+ kuthamangira kukachisiko. Kenako anagwira Paulo ndi kumukokera kunja kwa kachisi.+ Nthawi yomweyo zitseko zinatsekedwa. 31 Ndipo pamene anali kufuna kumupha, uthenga unafika kwa mtsogoleri wa gulu la asilikali kuti mu Yerusalemu monse muli chisokonezo.+ 32 Mwamsanga, iye anatenga asilikali ndi akapitawo awo ndi kuthamangira kumeneko.+ Anthuwo ataona mkulu wa asilikali+ uja pamodzi ndi asilikali akewo, analeka kumenya Paulo.
33 Pamenepo mkulu wa asilikali uja anafika pafupi ndi kumugwira ndipo analamula kuti amumange ndi maunyolo awiri.+ Ndiyeno anafunsa za iye kuti anali ndani ndiponso zimene anachita. 34 Koma ena m’khamulo anayamba kufuula zinthu zina, enanso zina.+ Choncho, atalephera kutolapo mfundo yeniyeni chifukwa cha phokoso, analamula kuti apite naye kumpanda wa asilikali.+ 35 Ndiyeno atafika pamasitepe, asilikaliwo anachita kumunyamula chifukwa chakuti khamulo linali kuchita chiwawa. 36 Khamu la anthu linali kuwatsatira, likufuula kuti: “Aphedwe ameneyo!”+
37 Koma atatsala pang’ono kulowa naye kumpanda wa asilikali, Paulo anauza mkulu wa asilikali kuti: “Mungandilole kodi kulankhula nanu pang’ono?” Iye anati: “Kodi umalankhula Chigiriki? 38 Kodi si iwe Mwiguputo uja amene masiku apitawo unayambitsa chipolowe choukira boma+ ndi kutsogolera zigawenga 4,000 kupita nazo m’chipululu?” 39 Pamenepo Paulo ananena kuti: “Inetu ndine Myuda+ wa ku Tariso,+ ku Kilikiya, nzika ya mzinda wotchuka. Chonde ndikukupemphani, kuti mundilole ndilankhule kwa anthuwa.” 40 Atamulola, Paulo anaimirira pamasitepe ndi kukwezera anthuwo dzanja.+ Onse atakhala phee, analankhula nawo m’Chiheberi,+ kuti: